30 Ndipo wansembe apereke limodzi likhale nsembe yaucimo, ndi linalo likhale nsembe yopsereza; ndipo wansembe amcitire comtetezera pamaso pa Yehova cifukwa ca kukha kwace komdetsa.
31 Motero muzipatula ana a Israyeli kwa kudetsedwa kwao; angafe m'kudetsedwa kwao, pamene adetsa kacisi wanga ali pakati pao.
32 Ici ndi cilamulo ca wakukha, ndi ca iye wakugona uipa, kuti kumkhalitse wodetsedwa;
33 ndi ca mkazi alinkudwala ndi kudetsedwa kwace, ndi ca iye alikukha kapena mwamuna, kapena mkazi, ndi ca iye agona ndi mkazi wodetsedwa.