10 Usamabvula mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wako, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wako; pakuti thupi lao ndi lako.
11 Usamabvula mwana wamkazi wa mkazi wa atate wako, amene anambala atate wako, ndiye mlongo wako.
12 Usamabvula mlongo wa atate wako; ndiye wa cibale ca atate wako.
13 Usamabvula mbale wa mai wako; popeza ndiye mbale wa mai wako.
14 Usamabvula mbale wa atate wako; usamasendera kwa mkazi wace; ndiye mai wako.
15 Usamabvula mpongozi wako; ndiye mkazi wa mwana wamwamuna wako; usamambvula.
16 Usamabvula mkazi wa mbale wako; ndiye thupi la mbale wako.