3 ndi cifukwa ca mlongo wace weni weni, akakhala namwali wosakhala naye mwamuna, nkuloleka adzidetse cifukwa ca iwowa.
4 Akakhala mwini banja pakati pa anthu a mtundu wace, asadzidetse, ndi kudziipsa,
5 Asamete tsitsi la pamtu pao, kapena kucecerera ndebvu zao, kapena kudziceka matupi ao.
6 Azikhala opatulikira Mulungu wao, osaipsa dzina la Mulungu wao; popeza amapereka nsembe zamoto za Yehova, mkate wa Mulungu wao; cifukwa cace akhale opatulika.
7 Asadzitengere mkazi wacigololo, kapena woipsidwa; asatenge mkazi woti adamcotsa mwamuna wace; popeza apatulikira Mulungu wace.
8 Cifukwa cace umpatule; popeza amapereka mkate wa Mulungu wako; umuyese wopatulika; pakuti Ine Yehova wakupatula iwe, ndine woyera,
9 Akadziipsa mwana wamkazi wa wansembe ndi kucita cigololo, alikuipsa atate wace; amtenthe ndi moto.