23 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
24 Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku loyamba la mweziwo, muzipumula, ndiko cikumbutso ca kuliza malipenga, msonkhano wopatulika.
25 Musamagwira nchito ya masiku ena; mubwere nayo nsembe yamoto ya Yehova.
26 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
27 Komatu, tsiku lakhumi la mwezi uwu wacisanu ndi ciwiri, ndilo tsiku la citetezero; mukhale nao msonkhano wopatulika, ndipo mudzicepetse; ndi kubwera nayo nsembe yamoto kwa Yehova.
28 Musamagwira nchito iri yonse tsiku limenelo; pakuti ndilo tsiku la citetezero, kucita cotetezera inu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Pakuti munthu ali yense wosadzicepetsa tsiku limenelo, amsadze kwa anthu a mtundu wace.