5 Ndipo wansembe wodzozedwayo atengeko mwazi wa ng'ombeyo, nabwerenao ku cihema cokomanako;
6 ndipo wansembeyo abviike cala cace m'mwazimo, nawaze mwaziwo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova cakuno ca nsaru yocinga, ya malo opatulika.
7 Ndipo wansembeyo atengeko mwazi, nauike pa nyanga za guwa la nsembe la cofukiza ca pfungo lokoma, lokhala m'cihema cokomanako pamaso pa Yehova; nathire mwazi wonse wa ng'ombeyo patsinde pa guwa la nsembe yopsereza, lokhala pa khomo la cihema cokomanako.
8 Ndipo acotse mafuta onse a ng'ombe ya nsembe yaucimo, acotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,
9 ndi imso ziwiri ndi mafuta ali pomwepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso,
10 umo azikacotsera pa ng'ombe ya nsembe yoyamika; ndipo wansembe azitenthe pa guwa la nsembe yopsereza.
11 Naturutse cikopa ca ng'ombeyo, ndi nyama yace yonse, pamodzi ndi mutu wace, ndi miyendo yace, ndi matumbo ace, ndi cipwidza cace,