1 Ndipo cilamulo ca nsembe yoparamula ndi ici: ndiyo yopatulikitsa.
2 Pamalo pophera nsembe yopsereza ndipo aziphera nsembe yoparamula; nawaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.
3 Ndipo acotseko, nabwere nao mafuta ace onse; mcira wamafuta, ndi mafuta akukuta matumbo,
4 ndi imso ziwiri, ndi mafuta a pamenepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso;
5 ndipo wansembe atenthe izi pa guwa la nsembe, nsembe yamoto ya kwa Yehova; ndiyo nsembe yoparamula.