14 Pamene anafika ku Leki Afilisti anapfuula pokomana naye; koma mzimu wa Yehova unamgwera kolimba, ndi zingwe zokhala pa manja ace zinanga bwazi lopserera ndi moto, ndi zomangira zace zinanyotsoka pa manja ace.
15 Ndipo anapeza cibwano catsopano ca buru, natambasula dzanja lace nacigwira, nakantha naco amuna cikwi cimodzi.
16 Nati Samsoni,Ndi cibwano ca buru, miuru miuru,Amuna cikwi ndawakantha ndi cibwano ca buru.
17 Ndipo kunali, atatha kunena, anataya cibwano m'dzanja lace; nawacha maiowo Ramati-leki ndiko kunena citunda ca cibwano.
18 Ndipo anamva ludzu lambiri, naitana kwa Yehova, nati, Mwapatsa Inu cipulumutso ici cacikuru ndi dzanja la kapolo wanu; ndipo kodi ndife nalo ludzu tsopano ndi kugwa m'dzanja la osadulidwa awa?
19 Pamenepo Mulungu anang'amba pokumbika paja pit Leki, naturukamo madzi; namwa iye, nubwera moyo wace, natsitsimuka iye; cifukwa cace anawacha dzina lace, Kasupe wa wopfuula, ndiwo m'Leki mpaka lero lino.
20 Ndipo Samsoni anaweruza Israyeli m'masiku a Afilisti zaka makumi awiri.