5 Koma munthuyu Mika anali nayo nyumba ya milungu, napanga cobvala ca wansembe, ndi timafano, namninkha zansembe mwana wace wina wamwamuna, amene anakhala wansembe wace.
6 Masikuwa panalibe mfumu m'Israyeli, yense anacita comuyenera m'maso mwace.
7 Ndipo panali mnyamata wa ku Betelehemu-Yuda wa banja la Yuda, ndiye Mlevi, nagonera iye komweko.
8 Adacokera munthuyo m'mudzi m'Betelehemu-Yuda, kugonera pali ponse akapeza pokhala; ndi pa ulendo wace anafika ku mapiri a Efraimu, ku nyumba ya Mika.
9 Ndipo Mika ananena naye, Ufumira kuti? Nati kwa iye, Ndine Mlevi wa ku Betelehemu-Yuda, ndirikumuka kugonera kumene ndikapeza pokhala.
10 Nanena naye Mika, Khalitsa nane, nukhale atate wanga, ndi wansembe wanga, ndipo ndidzakupatsa ndarama khumi pacaka, ndi cobvala cofikira, ndi zakudya zako. Nalowa Mleviyo.
11 Ndi Mleviyo anabvomera kukhalitsa ndi munthuyo; ndi mnyamatayo anamkhalira ngati mmodzi wa ana ace.