6 Ndipo ana a Israyeli anamva cifundo cifukwa ca Benjamini mbale wao, nati, Pfuko limodzi lalikhidwa pa Israyeli leroli.
7 Tidzatani kuwafunira otsalawo akazi, popeza tinalumbira ife pa Yehova kuti sitidzawapatsa ana athu akazi akhale akazi ao?
8 Nati iwo, Kodi pali lina la mapfuko a Israyeli losakwera kudza kwa Yehova ku Mizipa? Ndipo taonani, kucokera ku Yabesi-gileadi sanadza mmodzi kumisasa, kumsonkhano.
9 Pakuti pamene anawerenga anthu, taonani, panalibe mmodzi komweko wa okhala m'Yabesi-gileadi,
10 Ndipo msonkhano unatumizako amuna zikwi khumi ndi ziwiri, ndiwo ngwazi, nawalamulira ndi kuti, Mukani, nimuwakanthe okhala m'Yabesi-gileadi ndi lupanga lakuthwa, ndi akazi ndi ana ang'ono.
11 Ndipo cimene mukacite ndi ici: mukaononge konse mwamuna ali yense, ndi mkazi ali yense wodziwa mwamuna mogona naye.
12 Ndipo anapeza mwa anthu a Yabesi-gileadi anamwali mazana anai osadziwa mwamuna mogona naye; nabwera nao kumisasa ku Silo, ndiwo a m'dziko la Kanani.