15 mpaka Yehova atapatsa abale anu mpumulo, monga umo anakuninkhirani inu, naonso alandira dzikolo awaninkha Yehova Mulungu wanu; pamenepo mubwerere ku dziko lanu lanu, ndi kukhala nalo, limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya lino la Yordano la kum'mawa,
16 Ndipo anamyankha Yoswa, nati, Zonse mwatilamulira tidzacita, ndipo kuli konse mutitumako tidzamuka.
17 Monga momwe tinamvera mau onse a Mose momwemo tidzamvera inu; komatu akhale ndi inu Yehova Mulungu wanu monga anakhala ndi Mose.
18 Ali yense wakupikisana ndi inu, osamvera mau anu muli monse mukamlamulira, aphedwe; komatu khalani wamphamvu, nimulimbike mtima.