34 Ndipo anapatsa kwa mabanja a ana a Merari, otsala a Alevi, motapira pa pfuko la Zebuloni, Yokineamu ndi mabusa ace, ndi Karita ndi mabusa ace,
35 Dimna ndi mabusa ace, Nahalala ndi mabusa ace; midzi inai.
36 Ndipo motapira pa pfuko la Rubeni, Bezeri ndi mabusa ace, ndi Yahazi ndi mabusa ace,
37 Kedimotu ndi mabusa ace, ndi Mefati ndi mabusa ace; midzi inai.
38 Ndipo motapira m'pfuko la Gadi, Ramoti m'Gileadi ndi mabusa ace ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Mahanaimu ndi mabusa ace;
39 Hesiboni ndi mabusa ace. Yazeri ndi mabusa ace: yonse pamodzi midzi inai.
40 Yonseyi ndiyo midzi ya ana a Merari monga mwa mabanja ao, ndiwo otsala a mabanja a Alevi; ndipo gawo lao ndilo midzi khumi ndi iwiri.