1 Koma ku Yeriko anatseka pazipata, natsekedwa cifukwa ca ana a Israyeli, panalibe woturuka, panalibenso wolowa.
2 Ndipo Yehova ananena kwa Yoswa, Taona, ndapereka m'dzanja lako Yeriko ndi mfumu yace, ndi ngwazi zace.
3 Ndipo muzizungulira mudzi Inu nonse ankhondo, kuuzungulira mudzi kamodzi. Muzitero masiku asanu ndi limodzi.
4 Ndipo ansembe asanu ndi awiri azinyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga: za nkhosa zamphongo, natsogolere nazo likasa; koma tsiku lacisanu ndi ciwiri muzizungulira mudziwo kasanu ndi kawirio ndi ansembe aziliza mphalasazo.
5 Ndipo kudzakhala kuti akaliza cilizire ndi nyanga ya nkhosa yamphongo, nimumva kulira kwa mphalasa, anthu onse apfuule mpfuu yaikuru; ndipo linga la mudziwo lidzagwa pomwepo, ndi anthu adzakwera ndi kulowamo yense kumaso kwace.