2 anasonkhana kuponyana ndi Yoswa ndi Israyeli, ndi mtima umodzi.
3 Koma pamene nzika za Gibeoni zinamva zimene Yoswa adacitira Yeriko ndi Ai,
4 zinacita momcenierera, nizimuka nizioneka ngati mithenga, nizitenga matumba akale pa aburu ao, ndi matumba a vinyo akale ndi ong'ambika ndi omangamanga;
5 ndi nsapato zakale za zigamba pa mapazi ao, nizibvala nsanza; ndi mikate yonse ya kamba wao inali youma ndi yoyanga nkhungu.
6 Ndipo zinamuka kwa Yoswa kumisasa ku Giligala, niziti kwa iye ndi kwa amuna a Israyeli, Tacokera dziko lakutali, cifukwa cace mupangane nafe.
7 Ndipo amuna a Israyeli anati kwa Ahivi, Kapena mulimkukhala pakati pa ife, ndipo tipanganenji ndi inu?
8 Koma anati kwa Yoswa, Ndife akapolo anu. Pamenepo Yoswa anati kwa iwo, Ndinu ayani? ndipo mufuma kuti