9 Ndipo anati kwa iye, Akapolo anu afumira dziko la kutalitali, cifukwa lea dzina la Yehova Mulungu wanu; pakuti tidamva mbiri yace, ndi zonse anacita m'Aigupto,
10 ndi zonse anacitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya lija la Yordano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya ku Basana wokhala ku Asitorotu.
11 Ndipo akuru athu ndi nzika zonse za m'dziko mwathu zidanena nafe ndi kuti, Mutenge m'dzanja lanu kamba wa paulendo, kakomane naoni, nimunene nao, Ndife akapolo anu; ndipo tsopano mupangane nafe.
12 Mkate wathu uwu tinadzitengera kamba m'nyumba zathu, ukali wamoto, tsiku loturuka Ife kudza kwanu kuno; koma tsopano, taonani, uli wouma ndi woyaoga nkhungu;
13 ndi matumba a vinyo awa tinawadzaza akali atsopano; ndipo taonani, ang'ambika; ndi malaya athu awa ndi nsapato zathu zatha, cifukwa ca ulendo wocokera kutali ndithu.
14 Pamenepo amunawo analandirako kamba wao, osafunsira pakamwa pa Yehova.
15 Ndipo Yoswa anacitirana nao mtendere, napangana nao, akhale amoyo; ndi akalonga a msonkhano anawalumbirira,