36 Koma kasupe kapena citsime muli madzi, zidzakhala zoyera; koma iye amene akhudza mitembo yao adzadetsedwa.
37 Ndipo kanthu ka mtembo wace kakagwa pa mbeu yofesa, ikati ifesedwe, idzakhala yoyera.
38 Koma akathira madzi pa mbeuyi, ndi kanthu ka mtembo wace kakagwapo, muiyese yodetsedwa.
39 Ndipo ikafa nyama yakudya, iye amene akhudza mtembo wace adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
40 Ndipo iye wakudya kanthu ka mtembo wace azitsuka zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; iyenso wakunyamula mtembo wace atsuke zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
41 Ndipozokwawazonsezakukwawa pa dziko lapansi zikhale zonyansa; musamazidya.
42 Zonse zoyenda cafufumimba, ndi zonse za miyendo inai, kapena zonse zokhala nayo miyendo yambiri ndi zokwawa zonse zakukwawa pansi, musamazidya; popeza ndizo zonyansa.