33 pamenepo azimeta, koma osameta pamfundu; ndipo wansembe ambindikiritse iye wamfundu masiku asanu ndi awiri ena;
34 ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri aone mfunduyo; ndipo taonani, ngati mfundu njosakula pakhungu, ndipo ioneka yosakula kubzola khungu, wansembe amuche woyera, ndipo iye atsuke zobvala zace, nakhala woyera.
35 Koma ngati mfundu ikula pakhungu atachedwa woyera;
36 pamenepo wansembe amuone, ndipo taonani, ngati mfundu yakula pakhungu, wansembe asafunefune tsitsi loyezuka, ndiye wodetsedwa.
37 Koma monga momwe apenyera iye, ngati mfundu yaima pomwe, ndipo pamera tsitsi lakuda, mfundu yapola, ndiye woyera, ndipo wansembe amuche woyera.
38 Ndipo ngati mwamuna kapena mkazi ali ndi zikanga pa khungu la thupi lace, zikanga zoyerayera;
39 wansembe aziona; ndipo taonani ngati zikanga ziri pa khungu la thupi lao zikhala zotuwatuwa; ndilo thuza labuka pakhungu; ndiye woyera.