56 Ndipo wansembe akaona, ndipo taonani, nthenda yazimba ataitsuka, pamenepo aikadzule pa cobvala, kapena cikopa, kapena muyaro, kapena mtsendero;
57 ndipo ikaonekabe pacobvala, ngakhale pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, irikubukanso; ucitenthe ndi moto cija canthenda.
58 Ndipo ukatsuka cobvalaco, kapena muyaro, kapena mtsendero, kapena cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, ngati nthenda yalekapo pa cimeneco, acitsukenso kawiri, pamenepo ciri coyera.
59 Ici ndi cilamulo ca nthenda yakhate iri pa cobvala caubweya kapena cathonje, ngakhale pamuyare, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa; kucicha coyera kapena kucicha codetsa.