1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Nena ndi Aroni, ndi ana ace amuna, ndi ana a Israyeli onse, nuti nao, Ici ndi cimene Yehova wauza, ndi kuti,
3 Munthu ali yense wa mbumba ya Israyeli akapha ng'ombe, kapena mwana wa nkhosa, kapena mbuzi, m'cigono, kapena akaipha kunja kwa cigono,
4 osadza nayo ku khomo la cihema cokomanako, kuti aipereke copereka ca Yehova, ku bwalo la kacisi wa Yehova; azimuyesa munthuyu wocimwira mwazi, wakhetsa mwazi; ndipo amsadze munthuyo kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace;