6 Asasendere mmodzi wa inu kwa mbale wacekumbvula; Ine ndine Yehova.
7 Usamabvula atate wako, ndi mai wako; ndiye mai wako, usamambvula.
8 Usamabvula mkazi wa atate wako; ndiye thupi la atate wako.
9 Usamabvula mlongo wako, mwana wamkazi wa atate wako, kapena mwana wamkazi wa mai wako, wobadwa kwanu, kapena wobadwa kwina.
10 Usamabvula mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wako, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wako; pakuti thupi lao ndi lako.
11 Usamabvula mwana wamkazi wa mkazi wa atate wako, amene anambala atate wako, ndiye mlongo wako.
12 Usamabvula mlongo wa atate wako; ndiye wa cibale ca atate wako.