25 Caka cacisanu muzidya zipatso zace, kuti zobala zace zikucurukireni inu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26 Musamadya kanthu ndi mwazi wace; musamacita nyanga, kapena kuombeza ula.
27 Musamameta mduliro, kapena kusenga m'mphepete mwa ndebvu zanu,
28 Musamadziceka matupi anu cifukwa ca akufa, kapena kutema mpbini; Ine ndine Yehova.
29 Usamaipsa mwana wako wamkazi ndi kumcititsa cigololo; lingadzale ndi cigololo dzikoli, ndi kudzazidwa nazo zocititsa manyazi.
30 Muzisunga masabata anga, ndi kucitira ulemu malo anga opatulika; Ine ndine Yehova.
31 Musamatembenukira kwa obwebweta, kapena anyanga; musawafuna, ndi kudetsedwa nao; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.