29 Pakuti munthu ali yense wosadzicepetsa tsiku limenelo, amsadze kwa anthu a mtundu wace.
30 Ndi munthu ali yense wakugwira nchito iri yonse tsiku limenelo, ndidzaononga munthuyo pakati pa anthu a mtundu wace.
31 Musamagwira nchito iri yonse; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu, m'nyumba zanu zoo nse.
32 Likhale ndi inu Sabata lakupumula; ndipo mudzicepetse; tsiku lacisanu ndi cinai madzulo, kuyambira madzulo kufikira madzulo musunge Sabata lanu.
33 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
34 Nena ndi ana a Israyeli, kuti, Tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uno wacisanu ndi ciwiri pali madyerero a misasa a Yehova, masiku asanu ndi awiri.
35 Tsiku loyamba likhale msonkhano wopatulika, musamagwira nchito ya masiku ena.