51 Zikamtsalira zaka zambiri, monga mwa izi abwezere ndarama zakumuombola zocokera ku ndalama zomgulazo.
52 Ndipo zikamtsalira zaka pang'ono kufikira caka coliza lipenga amwerengere; monga mwa zaka zace abwezere mtengo wace wakumuombola.
53 Akhale naye monga wolipidwa caka ndi caka; asamamlamulira momzunza pamaso pako,
54 Ndipo akapanda kumuombola motero, azituruka caka coliza lipenga, iye ndi ana ace omwe.
55 Pakuti ana a Israyeli ndi atumiki anga; iwo ndiwo atumiki anga amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.