4 ndi imso ziwiri, ndi mafuta ali pomwepo okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso.
5 Ndipo ana a Aroni azitenthe pa guwa la nsembe, pa nsembe yopsereza, iri pa nkhuni zimene ziri pamoto; ndiyo nsembe yamoto, ya pfungo lokoma la kwa Yehova.
6 Ndipo copereka cace cikakhala nkhosa kapena mbuzi, kuti ikhale nsembe yoyamika ya kwa Yehova; ingakhale yaimuna kapena yaikazi, azibwera nayo yopanda cirema;
7 akabwera nayo nkhosa kuti ikhale copereka cace, abwere nayo pamaso pa Yehova;
8 naike dzanja lace pamutu pa copereka cace, naiphe patsogolo pa cihema cokomanako; ndipo ana a Aroni awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.
9 Pamenepo abwere nayo nsembe yamoto ya kwa Yehova; yotengako ku nsembe yoyamika; mafuta ace, mcira wamafuta wonse, ataucotsa kufupi ku pfupa lao msana; naicotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,
10 ndi imso ziwiri, ndi mafuta ali pomwepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso.