1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Tenga Aroni ndi ana ace pamodzi naye ndi zobvalazo, ndi mafuta odzozawo, ndi ng'ombe ya nsembe yaucimoyo, ndi nkhosa zamphongo ziwirizo, ndi mtanga wa mkate wopanda cotupitsawo;
3 nusonkhanitse khamu lonse ku khomo la cihema cokomanako.
4 Ndipo Mose anacita monga Yehova anamuuza; ndi khamulo linasonkhana pa khomo la cihema cokomanako.
5 Ndipo Mose anati kwa msonkhanowo, Ici ndi cimene Yehova adauza kuti cicitike.
6 Ndipo Mose anabwera nao Aroni ndi ana ace, nawasambitsa ndi madzi,