1 Koma ana a Israyeli anacita coipa pamaso pa Yehova; ndipo Yehova anawapereka m'dzanja la Midyani zaka zisanu ndi ziwiri.
2 Pamene dzanja la Midyani linalaka Israyeli, ana a Israyeli anadzikonzera ming'ang'ala ya m'mapiri, ndi mapanga, ndi malinga cifukwa ca Midyani.
3 Ndipo kunali, akabzala Israyeli, amakwera Amidyani, ndi Amaleki, ndi ana a kum'mawa, inde amawakwerera;
4 nawamangira misasa, namaononga zipatso za m'dziko mpaka ufika ku Gaza, osawasiyira cocirira njala m'Israyeli, ngakhale nkhosa, kapena ng'ombe, kapena buru.
5 Pakuti anakwera nazo zoweta zao ndi mahema ao, analowa ngati dzombe kucuruka kwao; iwowa ndi ngamila zao zomwe nzosawerengeka; ndipo analowa m'dziko kuliononga.
6 Ndipo Israyeli anafoka kwambiri cifukwa ca Midyani; ndipo ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova.
7 Ndipo kunali, pamene ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova cifukwa ca Midyani,