25 Ndipo mfumu Solomo anatuma dzanja la Benaya mwana wa Yehoyada, ndipo anamgwera, namwalira iye.
26 Ndipo mfumu inanena ndi Abyatara wansembeyo, Pita ku Anatoti ku minda yako; pakuti wakutidwa ndi imfa; koma sindikupha iwe lero lino, cifukwa unanyamula likasa la Ambuye Yehova pamaso pa Davide atate wanga, ndi popeza unazunzidwa monse umo atate wanga Davide anazunzidwamo.
27 Motero Solomo anacotsa Abyatara asakhalenso wansembe wa Yehova, kuti akakwaniritse mau a Yehova amene aja adalankhula ku Silo za mbumba ya Eli.
28 Ndipo mbiriyi inamfika Yoabu, pakuti Yoabu anapambukira kwa Adoniya, angakhale sanapambukira kwa Abisalomu. Ndipo Yoabu anathawira ku cihema ca Yehova, nagwira nyanga za guwa la nsembe.
29 Ndipo anamuuza mfumu Solomo, kuti, Yoabu wathawira ku cihema ca Yehova; ndipo taonani, wakhala ku guwa la nsembe. Pomwepo Solomo anatuma Benaya mwana wa Yehoyada, nati, Kamkwereo
30 Nafika Benaya ku cihema ca Yehova, nati kwa iye, Mfumu itero, Taturuka. Nati, Iai, koma ndifere pompano. Ndipo Benaya anabweza mau kwa mfumu, nati, Yoabu wanena cakuti, nandiyankha mwakuti mwakuti.
31 Ndipo mfumu inati kwa iye, Cita monga umo wanena iye, numkwere, numuike; kuti undicotsere ine ndi nyumba ya atate wanga mwazi uja Yoabu anaukhetsa wopanda cifukwa.