18 Ndipo pamene thupi liri ndi cironda pakhungu pace, ndipo capola,
19 ndipo padali cironda pali cotupa coyera, kapena cikanga cotuuluka, pamenepo acionetse kwa wansembe; ndipo wansembe aone,
20 ndipo taonani, ngati cioneka cakumba kubzola khungu, ndipo tsitsi lace lisanduka lotuwa, pamenepo wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo nthenda yakhate yabuka m'cirondamo.
21 Koma wansembe akaciona, ndipo taonani, palibe tsitsi loyera pamenepo, ndipo sicinakumba kubzola khungu, koma cazimba, pamenepo wansembe ambindikiritse masiku asanu ndi awiri;
22 ndipo ngati capitirira khungu, wansembe amuche wodetsedwa; ndilo khate.
23 Koma ngati cikanga caima pomwepo, cosakula, ndico cipsera ca cironda; ndipo wansembe amuche woyera.
24 Kapena pamene thupi lidapsya ndi mota pakhungu pace, ndipo mnofu wofiira wakupsyawo usanduka cikanga cotuuluka, kapena cotuwa: