4 Koma ngati cikanga cikhala cotuwa pa khungu la thupi lace, ndipo cikaoneka cosapitirira khungu, ndi tsitsi lace losasanduka loyera, pamenepo wansembe ambindikiritse wanthendayo masiku asanu ndi awiri;
5 ndipo wansembe amuonenso tsiku lacisanu ndi ciwiri; ndipo taonani, monga momwe apenyera iye, nthenda yaima, nthenda siinapitirira pakhungu, pamenepo wansembe ambindikiritsenso masiku asanu ndi awiri ena;
6 ndipo wansembe amuonenso tsikulacisanu ndi ciwiri, ndipo taonani, nthenda yazimba yosapitirira khungu nthendayi, pamenepo wansembe amuche iye woyera, ndiyo nkhanambo cabe; ndipo atsuke zobvala zace, ndiye woyera;
7 koma nkhanambo ikapitirira khungu, atadzionetsakwa wansembe kuti achedwe woyera, adzionetsenso kwa wansembe;
8 ndipo wansembe aone, ndipo taonani, ngati nkhanambo yapitirira khungu, wansembe amuche wodetsedwa, ndilo khate.
9 Pamene nthenda yakhate iri mwa munthu, azimfikitsa kwa wansembe;
10 ndipo wansembe aone, ndipo taonani, ngati pali cotupa coyera pakhungu, ndipo casanduliza tsitsi likhale loyera, ndipo pacotupa pali mnofu wofiira,