11 Pakuti moyo wa nyama ukhala m'mwazi; ndipo ndakupatsani uwu pa guwa la nsembe, ucite cotetezera moyo wanu; pakuti wocita cotetezera ndiwo mwazi, cifukwa ca moyo wace.
12 Cifukwa cace ndinanena kwa ana a Israyeli, Asamadya mwazi mmodzi yense wa inu, kapena mlendo ali yense wakugoneramwa inu asamadya mwazi.
13 Ndipo munthu ali yense wa ana a Israyeli, kapena mlendo wakugonera pakati pa inu, akasaka nyama kapena mbalame yakudya, nakaigwira; azikhetsa mwazi wace naufotsere ndi dothi.
14 Pakuti ndiwo moyo wa: nyama zonse, mwazi wace ndiwo moyo wace; cifukwa cace ndinanena kwa ana a Israyeli, Musamadya mwazi wa nyama iri yonse; pakuti moyo wa nyama yonse ndi mwazi wace; ali yense akaudya adzasadzidwa.
15 Ndipo ali yense wakudya yakufa yokha, kapena yojiwa kuthengo, ngakhale ndiye wa m'dziko kapena mlendo, azitsuka nsaru zace, nasambe ndi madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; pamenepo adzakhala woyera.
16 Koma akapanda kuzitsuka, kapena kusamba thupi lace, adzasenza mpholupulu yace.