18 Usamtenga mkazi kumuonjezera kwa mbale wace, kumbvuta, kumbvula pamodzi ndi mnzace, akah ndi moyo mnzaceyo.
19 Usamasendera kwa mkazi kumbvula pokhala ali padera cifukwa ca kudetsedwa kwace.
20 Usagona naye mkazi wa mnansi wako, kudetsedwa naye limodzi.
21 Ndipo usamapereka a mbumba yako kuwapitiriza kumoto cifukwa ca Moleke, usamaipsa dzina la Mulungu wako: Ine ndine Yehova.
22 Usamagonana ndi mwamuna, monga amagonana ndi mkazi; conyansa ici.
23 Ndipo usamagonana ndi nyama iri yonse, kudetsedwa nayo; kapena mkazi asamaima panyama, kugonana nayo; cisokonezo coopsa ici.
24 Musamadzidetsa naco cimodzi ca izi; pakuti amitundu amene ndiwapitikitsa pamaso panu amadetsedwa nazo zonsezi;