21 Ndipo adze nayo nsembe yace yoparamula kwa Yehova, ku khomo la cihema cokomanako, ndiyo nkhosa yamphongo ikhale nsembe yoparamula.
22 Ndipo wansembe acite comtetezera ndi nkhosa yamphongo ya nsembe yoparamula pamaso pa Yehova, cifukwa ca kucimwa adacimwaku; ndipo adzakhululukidwa cifukwa ca kucimwa kwace adacimwaku.
23 Ndipo mukadzalowa m'dzikomo, ndi kubzalamitengo yamitundumitundu ikhale ya cakudya, muziyese zipatso zao monga kusadulidwa kwao; zaka zitatu muziyese zosadulidwa; zisadyedwa.
24 Koma caka cacinai zipatso zace zonse zikhale zopatulika, za kumlemekeza nazo Yehova.
25 Caka cacisanu muzidya zipatso zace, kuti zobala zace zikucurukireni inu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26 Musamadya kanthu ndi mwazi wace; musamacita nyanga, kapena kuombeza ula.
27 Musamameta mduliro, kapena kusenga m'mphepete mwa ndebvu zanu,