17 Munthu akatenga mlongo wace, mwana wamkazi wa atate wace, kapena mwana wamkazi wa mai wace, nakaona thupi lace, ndi mlongoyo akaona thupi lace; cocititsa manyazi ici; ndipo awasadze pamaso pa ana a anthu ao; anabvula mlongo wace; asenze mphulupulu yace.
18 Munthu akagona ndi mkazi ali mumsambo, nakambvula, anabvula kasupe wace, ndi iye mwini anabvula kasupe wa nthenda yace; awadule onse awiri pakati pa anthu a mtundu wao.
19 Usamabvula mbale wa mai wako, kapena mlongo wa atate wako; popeza anabvula abale ace; asenze mphulupulu yao.
20 Munthu akagona ndi mkazi wa mbale wa atate wace, nabvula mbale wa atate wace; asenze kucimwa kwao; adzafa osaona ana.
21 Munthu akatenga mkazi wa mbale wace, codetsa ici; wabvula mbale wace; adzakhala osaona ana.
22 Potero muzisunga malemba anga onse, ndi maweruzo anga onse, kuwacita; lingakusanzeni inu dziko limene ndipita nanuko, kuti mukhale m'mwemo.
23 Musamatsata miyambo ya mtundu umene neliucotsa pamaso panu; popeza anacita izi zonse, nelinalema nao.