2 Unenenso kwa ana a Israyeli ndi kuti, Ali yense wa ana a Israyeli, kapena wa alendo akukhala m'Israyeli, amene apereka mbeu zace kwa Moleke, azimupha ndithu; anthu a m'dziko amponye miyala.
3 Ndipo nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndi kumsadza kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace; popeza anapereka a mbeu zace kwa Moleke, kudetsa nako malo anga opatulika, ndi kuipsa dzina langa lopatulika.
4 Ndipo ngati anthu a m'dzikomo akambisa munthuyo pang'ono ponse, pamene apereka a mbeu zace kwa Moleke, kuti asamuphe;
5 pamenepo nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndi banja lace, ndi kumsadza iye, ndi onse akumtsata ndi cigololo kukacita cigololo kwa Moleke, kuwacotsa pakati pa anthu a mtundu wao.
6 Ndipo munthu wakutembenukira kwa obwebweta ndi anyanga kuwatsata ndi cigololo, nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndipo ndidzamsadza kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace.
7 Cifukwa cace dzipatuleni, nimukhale oyera; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
8 Ndipo musunge malemba anga ndi kuwacita; Ine ndine Yehova wakupatula inu.