20 ndipo anaika mafuta pa ngangazo, natentha mafutawo pa guwa la nsembe.
21 Ndipo Aroni anaweyula ngangazo ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; monga iye anauza Mose.
22 Ndipo Aroni anakweza dzanja lace kulozera anthu, nawadalitsa; natsika kuja anapereka nsembe yaucimo, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zoyamika.
23 Ndipo Mose ndi Aroni analowa ku cihema cokomanako, naturuka, nadalitsa anthu; ndipo ulemero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.
24 Ndipo unaturuka mota pamaso ya Yehova, nunyeketsa nsembe yopsereza ndi mafuta pa guwa la nsembe; ndipo pakuciona anthu onse anapfuula, nagwa nkhope zao pansi.