35 Ndipo Yehova anakantha Benjamini pamaso pa Israyeli; ndi ana a Israyeli anawaononga a Benjamini tsiku lija amuna zikwi makumi awiri ndi zisanu, kudza zana limodzi; awa onse ndiwo akusolola lupanga.
36 Ndipo ana a Benjamini anaona kuti takanthidwa; popeza amuna a Israyeli anawapatsa Abenjamini malo, pakuti anatama olalira amene anawaikiratu pa Gibeya.
37 Nafulumira olalirawo nathamangira Gibeya, nabalalika olalirawo, nakantha mudzi wonse ndi lupanga lakuthwa.
38 Koma kunali cizindikilo coikika pakati pa amuna a Israyeli ndi olalirawo, ndico cakuti afukitse mtambo wa utsi kumudzi.
39 Ndi nkhondo ya Israyeli inathawa, ndipo Benjamini anayamba kuwakantha ndi kuwagwaza amuna a Israyeli, ngati amuna makumi atatu, pakuti anati, Ndithu Tawakantha konse pamaso pathu, monga ku nkhondo yoyambayo.
40 Koma pamene mtambo unayamba kukwera m'mudzi ngati utsi uti tolo, Abenjamini anaceuka, ndipo taonani, pamodzi ponse panafuka utsi kumwamba.
41 Natembenuka amuna a Israyeli; nadabwa amuna a Benjamini; popeza anaona kuti cidawagwera coipa.