14 Pamenepo anati, Nanga timcitire iye ciani? Nati Gehazi, Zedi alibe mwana, ndi mwamuna wace wakalamba.
15 Nati, Kamuitane. Namuitana, naima pakhomo mkaziyo.
16 Ndipo anati, Nyengo yino caka cikudzaci udzafukata mwana wamwamuna. Koma anati, lai, mbuyanga, munthu wa Mulungu, musanamiza mdzakazi wanu.
17 Ndipo mkaziyo anaima, naona mwana wamwamuna nyengo yomweyo caka cimene cija Elisa adanena naye.
18 Ndipo atakula mwanayo, linadza tsiku lakuti anaturuka kumka kwa atate wace, ali kwa omweta tirigu.
19 Natikwa atate wace, Mutu wanga, mutu wanga! Pamenepo anati kwa mnyamata, Umnyamule umuke naye kwa amace.
20 Namnyamula, napita naye kwa amace. Ndipo anakhala pa maondo ace kufikira usana, namwalira.