2 Mafumu 16 BL92

Ahazi mfumu ya Yuda

1 Caka cakhumi mphambu zisanu ndi ziwiri ca Peka mwana wa Remaliya Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda analowa ufumu wace.

2 Ahazi anali wa zaka makumi awiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi m'Yerusalemu; koma sanacita zoongoka pamaso pa Yehova Mulungu wace, ngati Davide kholo lace;

3 popeza anayenda m'njira ya mafumu a Israyeli, napititsanso mwana wace pamoto, monga mwa zonyansa za amitundu amene Yehova anawaingitsa pamaso pa ana a Israyeli.

4 Ndipo anaphera nsembe, nafukiza zonunkhira kumisanje, ndi kuzitunda, ndi patsinde pa mtengo uli wonse wogudira.

5 Pamenepo Rezini mfumu ya Aramu, ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israyeli, anakwera kumka ku Yerusalemu kukacita nkhondo, nammangira Ahazi misasa; koma sanakhoza kumgonjetsa.

6 Nthawi yomweyo Rezini mfumu ya Aramu anabwezera Elati kwa Aramu, napitikitsa Ayuda ku Elati; nadza Aaramu ku Elati, nakhala komweko kufikira lero lino.

7 Ndipo Ahazi anatuma mithenga kwa Tigilati Pilesere mfumu ya Asuri, ndi kuti, Ine ndine kapolo wanu ndi mwana wanu; kwerani, mudzandipulumutse m'dzanja la mfumu ya Aramu, ndi m'dzanja la mfumu ya Israyeli anandiukirawo.

8 Natenga Ahazi siliva ndi golidi wopezeka m'nyumba ya Yehova, ndi ku cuma ca nyumba ya mfumu, nazitumiza mtulo kwa mfumu ya Asuri.

9 Nimmvera mfumu ya Asuri, nikwera kumka ku Damasiko mfumu ya Asuri, niulanda, nipita nao anthu ace andende ku Kiri, nimupha Rezini.

Guwa la nsembe la ku Damasiko

10 Ndipo mfumu Ahazi anamuka ku Damasiko kukakomana ndi Tigilati Pilesere mfumu ya Asuri, naona guwa la nsembe linali ku Damasiko; natumiza mfumu Ahazi kwa Uriya wansembe cithunzithunzi cace, ndi cifanizo cace, monga mwa mamangidwe ace onse.

11 Ndipo Uriya wansembe anamanga guwa la nsembelo, monga mwa zonse anazitumiza mfumu Ahazi zocokera ku Damasiko; momwemo Uriya wansembe analimanga asanabwere mfumu ku Damasiko.

12 Atafika mfumu kucokera ku Damasiko, anapenya mfumu guwa la nsembelo, nayandikiza mfumu ku guwa la nsembelo, napereka nsembe pomwepo.

13 Nafukiza nsembe yace yopsereza ndi nsemba yace yaufa, natsanulira nsembe yace yothira, nawaza mwazi wa nsembe zace zamtendere pa guwa la nsembelo,

14 Nalicotsa guwa la nsembe lamkuwa linali pamasopa Yehova, nalicotsa kukhomo la nyumba pakati pa guwa la nsembe lace ndi nyumba ya Yehova, naliikakumpotokwa guwa la nsembe lace.

15 Ndipo mfumu Ahazi analamulira Uriya wansembe, kuti, Pa guwa la nsembe lalikuru uzifukiza nsembe yopsereza yam'mawa, ndi nsembe yaufa yamadzulo, ndi nsembe yopsereza ya mfumu, ndi nsembe yace yaufa, pamodzi ndi nsembe yopsereza ya anthu onse a m'dziko, ndi nsembe yao yaufa, ndi nsembe zao zothira; uziwaza pa ilo mwazi wonse wa nsembe yopsereza, ndi mwazi wonse wa nsembe yophera; koma guwa la nsembe lamkuwa ndi langa, lofunsira nalo.

16 Nacita Uriya wansembe monga mwa zonse adalamulira mfumu Ahazi.

17 Ndipo mfumu Ahazi anadula matsekerezo a maphaka, nacotsa mbiya pamwamba pao, natsitsa thawale pamwamba pa ng'ombe zamkuwa ziri pansi pace, naziika pa ciunda camiyala.

18 Nacotsa ku nyumba ya Yehova malo ophimbika a pa Sabata adawamanga kunyumba, ndi polowera mfumu pofuma kunja, cifukwa ca mfumu ya Asuri.

19 Macitidwe ena tsono adawacita Ahazi, salembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

20 Nagona Ahazi ndi makolo ace, namuika ndi makolo ace m'mudzi wa Davide; nakhala mfumu m'malo mwace Hezekiya mwana wace.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25