4 Ndipo ngati anthu a m'dzikomo akambisa munthuyo pang'ono ponse, pamene apereka a mbeu zace kwa Moleke, kuti asamuphe;
5 pamenepo nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndi banja lace, ndi kumsadza iye, ndi onse akumtsata ndi cigololo kukacita cigololo kwa Moleke, kuwacotsa pakati pa anthu a mtundu wao.
6 Ndipo munthu wakutembenukira kwa obwebweta ndi anyanga kuwatsata ndi cigololo, nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndipo ndidzamsadza kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace.
7 Cifukwa cace dzipatuleni, nimukhale oyera; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
8 Ndipo musunge malemba anga ndi kuwacita; Ine ndine Yehova wakupatula inu.
9 Pakuti ali yense wakutemberera atate wace kapena mai wace azimupha ndithu; watemberera atate wace kapena mai wace; mwazi wace ukhale pamutu pace.
10 Munthu akacita cigololo ndi mkazi wa mwini, popeza wacita cigololo ndi mkazi wa mnansi wace, awaphe nditho, mwamuna ndi mkazi onse awiri.