8 Pamenepo Aroni anasendera kufupi kwa guwa la nsembe, napha mwana wa ng'ombe wa nsembe yaucimo, ndiyo ya kwa iye yekha.
9 Ndipo ana a Aroni anasendera nao mwazi kwa iye; ndipo anabviika cala cace m'mwazimo naupaka pa nyanga za guwa la nsembe, nathira mwaziwo patsinde pa guwa la nsembe;
10 koma mafutawo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa za nsembe yaucimo, anazitentha pa guwa la nsembe; monga Yehova anauza Mose.
11 Ndipo anatentha ndi moto nyamayi ndi cikopa kunja kwa cigono.
12 Ndipo anapha nsembe yopsereza; ndi ana a Aroni anapereka mwaziwo kwa iye, ndipo anauwaza pa guwa la nsembe pozu ngulira.
13 Ndipo anapereka nsembe yopsereza kwa iye, ciwalo ciwalo, ndi mutu wace; ndipo anazitentha pa guwa la nsembe.
14 Ndipo anatsuka matumbo ndi miyendo, nazitentha pa nsembe yopsereza pa guwa la nsembe.