9 Ndipo ana a Aroni anasendera nao mwazi kwa iye; ndipo anabviika cala cace m'mwazimo naupaka pa nyanga za guwa la nsembe, nathira mwaziwo patsinde pa guwa la nsembe;
10 koma mafutawo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa za nsembe yaucimo, anazitentha pa guwa la nsembe; monga Yehova anauza Mose.
11 Ndipo anatentha ndi moto nyamayi ndi cikopa kunja kwa cigono.
12 Ndipo anapha nsembe yopsereza; ndi ana a Aroni anapereka mwaziwo kwa iye, ndipo anauwaza pa guwa la nsembe pozu ngulira.
13 Ndipo anapereka nsembe yopsereza kwa iye, ciwalo ciwalo, ndi mutu wace; ndipo anazitentha pa guwa la nsembe.
14 Ndipo anatsuka matumbo ndi miyendo, nazitentha pa nsembe yopsereza pa guwa la nsembe.
15 Ndipo anabwera naco copereka ca anthu, natenga mbuzi ya nsembe yaucimo ndiyo ya kwa anthu, naipha, naipereka nsembe yaucimo, monga yoyamba ija.