23 Watonza Yehova mwa mithenga yako, nuti, Ndi magareta anga aunyinji ndakwera pa misanje ya mapiri ku mbali zace za Lebano, ndipo ndidzagwetsa mikungudza yace yaitali, ndi mitengo yace yosankhika yar mlombwa, ndidzalowanso m'ngaka mwace mweni mweni, ku nkhalango zace za madimba.
24 Ndakapa, ndamwa madzi acilendo, ndi ku mapazi anga ndidzaphwetsa mitsinje yonse ya Aigupto,
25 Sunamva kodi kuti Ine ndinacicita kale lomwe, ndi kucipanga masiku akalekale? tsopano ndacifikitsa kuli iwe, uzikhala wakupasula imidzi yamalinga ikhale miunda ya mabwinja.
26 Cifukwa cace okhalamo ao anali ofok a manja, anaopsedwa, nacita manyazi, ananga udzu wa kuthengo, ndi msipu wauwisi, ndi udzu wa patsindwi, ndi tirigu wopserera asanakule.
27 Koma ndidziwa kukhala pansi kwako, ndi kuturuka kwako, ndi kulowa kwako, ndi kundizazira kwako.
28 Cifukwa ca kundizazira kwako, ndi popeza kudzikuza kwako kwandifikira m'makutu mwanga, ndidzakukowa ndi ngowe yanga m'mphuno mwako, ndi cam'kamwa canga m'milomo mwako; ndipo ndidzakubwezera pa njira unadzerayi.
29 Ndi ici ndi cizindikilo cako: caka cino mudzadya za mphulumukwa, ndi caka ca mawa za mankhokwe, ndi caka camkuca muzibzala ndi kukolola, muzioka minda yampesa ndi kudya zipatso zace.