1 Ndipo ana a aneneri anati kwa Elisa, Taonani tsono, pamalo tikhalapo ife pamaso panu paticepera
2 Mutilole tipite ku Yordano, tikatengeko, ali yense mtengo, tidzimangire malo komweko, tikhalepo, Nati, Mukani.
3 Ndipo wina anati, Mulole mupite nafe anyamata anu. Nati, Ndidzamuka.
4 Namuka nao, nafika ku Yordano, iwo natema mitengo.
5 Ndipo wina analinkudula mtengo nkhwangwa inagwa m'madzi; ndipo anapfuula, nati, Kalanga ine mbuyanga! popeza ojobwereka.
6 Nati munthu wa Mulungu, Yagwera pati? Namuonetsapo yagwera. Pamenepo anadula kamtengo, nakaponya pomwepo, nayandamitsa nkhwangwayo.