13 Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;
14 Udzacita nafe maere,Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;
15 Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;
16 Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.
17 Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;
18 Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.
19 Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,