Miyambi 12 BL92

1 Wokonda mwambo akonda kudziwa;Koma wakuda cidzudzulo apulukira.

2 Yehova akomera mtima munthu wabwino;Koma munthu wa ziwembu amtsutsa,

3 Munthu sadzakhazikika ndi udio,Muzu wa olungama sudzasunthidwa.

4 Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace;Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.

5 Maganizo a olungama ndi ciweruzo;Koma uphungu wa oipa unyenga.

6 Mau a oipa abisalira mwazi;Koma m'kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7 Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.

8 Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9 Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10 Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.

11 Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.

12 Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13 M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.

14 Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.

15 Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;Koma wanzeru amamvera uphungu.

16 Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;Koma wanzeru amabisa manyazi.

17 Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.

18 Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;Koma lilime la anzeru lilamitsa.

19 Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;Koma lilime lonama likhala kamphindi.

20 Cinyengo ciri m'mitima ya oganizira zoipa;Koma aphungu a mtendere amakondwa.

21 Palibe bvuto lidzagwera wolungama;Koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa,

22 Milomo yonama inyansa Yehova;Koma ocita ntheradi amsekeretsa.

23 Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;Koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.

24 Dzanja la akhama lidzalamulira;Koma wolesi adzakhala ngati kapolo,

25 Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu;Koma mau abwino aukondweretsa.

26 Wolungama atsogolera mnzace;Koma njira ya oipa iwasokeretsa.

27 Wolesi samaocha nyama yace anaigwira;Koma wolungama amalandira cuma copambana ca anthu.

28 M'khwalala la cilungamo muli moyo;M'njira ya mayendedwe ace mulibe imfa.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31