Miyambi 17 BL92

1 Nyenyeswa youma, pokhala mtendere,Iposa nyumba yodzala nyama yansembe, pali makangano.

2 Kapolo wocitamwanzeruAdzalamulira mwana wocititsa manyazi,Nadzagawana nao abale colowa.

3 Siliva ali ndi mbiya yosungunulira, golidi ali ndi ng'anjo;Koma Yehova ayesa mitima.

4 Wocimwa amasamalira milomo yolakwa;Wonama amvera lilime losakaza.

5 Wocitira ciphwete aumphawi atonza Mlengi;Wokondwera ndi tsoka sadzapulumuka cilango.

6 Zidzukulu ndizo korona wa okalamba;Ndipo ulemerero wa ana ndiwo atate ao.

7 Mlomo wangwiro suyenera citsiru;Ngakhale mlomo wonama suyenera kalonga ndi pang'ono ponse.

8 Wolandira cokometsera mlandu aciyesa ngale;Pali ponse popita iye acenjera.

9 Wobisa colakwa afunitsa cikondano;Koma wobwereza-bwereza mau afetsa ubwenzi.

10 Cidzudzulo cilowa m'kati mwa wozindikira,Kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

11 Woipa amafuna kupanduka kokha;Koma adzamtumizira mthenga wankhanza.

12 Kukomana ndi citsiru m'kupusa kwaceKuopsya koposa cirombo cocicotsera anace.

13 Wobwezera zabwino zoipa,Zoipa sizidzamcokera kwao.

14 Ciyambi ca ndeu cifanana ndi kutsegulira madzi;Tsono kupikisana kusanayambe tasiya makani.

15 Wokometsa mlandu wa wamphulupulu, ndi wotsutsa wolungama,Onse awiriwa amnyansa Yehova.

16 Kodi bwanji mtengo wogulira nzeru uli m'dzanja la citsiru,Popeza wopusa alibe mtima?

17 Bwenzi limakonda nthawi zonse;Ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

18 Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina,Napereka cikole pamaso pa mnzace.

19 Wokonda ndeu akonda kulakwa;Ndipo wotarikitsa khomo lace afunafuna kuonongeka.

20 Wokhota mtima sadzapeza bwinoNdipo mwini lilime lokhota adzagwa m'zoipa.

21 Wobala citsiru adzicititsa cisoni;Ndipo atate wa wopusa sakondwa.

22 Mtima wosekerera uciritsa bwinoKoma mzimu wosweka uphwetsa mafupa,

23 Munthu woipa alandira cokometsera mlandu coturutsa m'mfunga,Kuti apambukitse mayendedwe a ciweruzo.

24 Nzeru iri pamaso pa wozindikira;Koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.

25 Mwana wopusa acititsa atate wace cisoni,Namvetsa zowawa amace wombala.

26 Kulipiritsa wolungama sikuli kwabwino,Ngakhale kukwapula akuru cifukwa aongoka mtima.

27 Wopanda cikamwakamwa apambana kudziwa;Ndipo wofatsa mtima ali wanzeru.

28 Ngakhalecitsirucikatontholaaciyesa canzeru;Posunama ali wocenjera.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31