Miyambi 5 BL92

Acenjere naye mkazi woipa

1 Mwananga, mvera nzeru yanga;Cherera makutu ku luntha langa;

2 Ukasunge zolingalira,Milomo yako ilabadire zomwe udziwa.

3 Pakuti milomo ya mkazi waciwerewere ikukha uci;M'kamwa mwace muti see koposa mafuta.

4 Cimariziro cace ncowawa ngati civumulo,Ndi cakuthwa ngati lupanga lakuthwa konse konse.

5 Mayendedwe ace atsikira kuimfa;Mapazi ace aumirira kumanda;

6 Sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo;Mayendedwe ace adzandira dzandi dzandi osadziwa iye.

7 Ndipo tsopano ana, mundimvere,Musapatuke ku mau a m'kamwa mwanga.

8 Siyanitsa njira yako kutari kwa iyeyo,Osayandikira ku khomo la nyumba yace;

9 Kuti ungapereke ulemu wako kwa ena,Ndi zaka zako kwa ankhanza;

10 Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;

11 Ungalire pa cimariziro cako,Pothera nyama yako ndi thupi lako;

12 Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;

13 Ndipo sindinamvera mau a aphunzitsi anga;Ngakhale kucherera makutu kwa akundilanga mwambo!

14 Ndikadakhala m'zoipa zonse,M'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.

15 Imwa madzi a m'citsime mwako,Ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.

16 Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja,Ndi mitsinje ya madzi m'makwalala?

17 Ikhale ya iwe wekha,Si ya alendo okhala nawe ai.

18 Adalitsike kasupe wako;Ukondwere ndi mkazi wokula nayo.

19 Ngati mbawala yokonda ndi cinkhoma cacisomo,Maere ace akukwanire nthawi zonse;Ukodwe ndi cikondi cace osaleka.

20 Pakuti ukondwerenji, mwananga, ndi mkazi waciwerewere,Ndi kufungatira cifuwa ca mkazi wacilendo?

21 Pakuti njira za munthu ziri pamaso pa Yehova,Asinkhasinkha za mayendedwe ace onse.

22 Zoipazacezacezidzagwira woipa;Adzamangidwa ndi zingwe za ucimo wace.

23 Adzafa posowa mwambo;Adzasocera popusa kwambiri.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31