Miyambi 28 BL92

Mau olinganiza zosiyana

1 Woipaathawapalibewomthamangitsa;Koma olungama alimba mtima ngati mkango.

2 Pocimwa dziko akalonga ace acuruka;Koma anthu ozindikira ndi odziwa alikhazikikitsa nthawi yaikuru.

3 Munthu waumphawi wotsendereza osaukaAkunga mvula yamadzi yokokolola dzinthu.

4 Omwe asiya cilamulo atama oipa;Koma omwe asunga cilamulo akangana nao.

5 Oipa samvetsetsa ciweruzo;Koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

6 Waumphawi woyenda mwangwiroApambana ndi yemwe akhotetsa njira zace, angakhale alemera.

7 Wosunga cilamulo ndiye mwana wozindikira;Koma mnzao wa adyera acititsa atate wace manyazi.

8 Wocurukitsa cuma cace, pokongoletsa ndi phindu,Angokundikira yemwe acitira osauka cisoni.

9 Wopewetsa khutu lace kuti asamve cilamulo,Ngakhale pemphero lace linyansa.

10 Wosoceretsa oongoka mtima alowe m'njira yoipa,Adzagwa mwini m'dzenje lace;Koma angwiro adzalandira colowa cabwino.

11 Wolemera adziyesa wanzeru;Koma wosauka wozindikira aululitsa zace.

12 Posekera olungama pali ulemerero wambiri;Koma pouka oipa anthu amabisala.

13 Wobisa macimo ace sadzaona mwai;Koma wakuwabvomereza, nawasiya adzacitidwa cifundo.

14 Wodala munthu wakuopakosalekeza;Koma woumitsa mtima wace adzagwa m'zoipa.

15 Monga mkango wobangula ndi cirombo coyendayenda,Momwemo mfumu yoipa ya anthu osauka.

16 Kalonga wosowa nzeru apambana kusautsa;Koma yemwe ada cisiriro adzatanimphitsa moyo wace.

17 Woparamula mlandu wakupha munthu adzathawira kudzenje;Asamuletse.

18 Woyenda mwangwiro adzapulumuka;Koma wokhota m'mayendedwe ace adzagwa posacedwa.

19 Wolima munda wace zakudya zidzamkwanira;Koma wotsata anthu opanda pace umphawi udzamkwanira.

20 Munthu wokhulupirika ali ndi madalitso ambiri;Koma wokangaza kulemera sadzapulumuka cilango,

21 Cetera siliri labwino,Ngakhale kulakwa kuti ukadye kanthu.

22 Mwini diso lankhwenzule akangaza kulemera,Osadziwa kuti umphawi udzamfikira.

23 Adzamkomera mtima wodzudzula m'tsogolo mwace,Koposa wosyasyalika ndi lilime lace.

24 Wobera atate wace, pena amace, nati, Palibe kulakwa;Ndiye mnzace wa munthu wopasula.

25 Wodukidwa mtima aputa makangano;Koma wokhulupirira Yehova adzakula.

26 Wokhulupirira mtima wace wace ali wopusa;Koma woyenda mwanzeru adzapulumuka,

27 Wogawira aumphawi sadzasowa;Koma wophimba maso ace adzatembereredwa kwambiri.

28 Pouka oipa anthu amabisala;Koma pakufa amenewo olungama acuruka.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31