Miyambi 18 BL92

1 Wopanduka afunafuna niro cace,Nakangana ndi nzeru yonse yeniyeni.

2 Wopusa sakondwera ndi kuzindikira;Koma kungobvumbulutsa za m'mtima mwace.

3 Pakudza wamphulupulu padzanso kunyoza;Manyazi natsagana ndi citonzo.

4 Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya;Kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.

5 Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankhu sikuli kwabwino,Ngakhale kucitira cetera wolungama.

6 Milomo ya wopusa ifikitsa makangano;Ndipo m'kamwa mwace muputa kukwapulidwa.

7 M'kamwa mwa wopusa mumuononga,Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.

8 Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,Zotsikira m'kati mwa mimba.

9 Wogwira nchito mwaulesiNdiye mbale wace wa wosakaza.

10 Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;Wolungama athamangiramo napulumuka.

11 Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;Alingalira kuti ndico khoma lalitari.

12 Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;Koma cifatso citsogolera ulemu.

13 Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.

14 Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?

15 Mtima wa wozindikira umaphunzira;Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

16 Mtulo wa munthu umtsegulira njira,Numfikitsa pamaso pa akuru.

17 Woyamba kudzinenera ayang'anika wolungama;Koma mnzace afika namuululitsa zace zonse.

18 Ula uletsa makangano,Nulekanitsa amphamvu.

19 Kupembedza mbale utamcimwira nkobvuta,Kulanda mudzi wolimba nkosabvuta;Makangano akunga mipiringidzo ya linga.

20 Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m'kamwa mwace;Iye nadzakhuta phindu la milomo yace.

21 Lilime liri ndi mphamvu pa imfa ndi moyo;Wolikonda adzadya zipatso zace.

22 Wopeza mkazi apeza cinthu cabwino;Yehova amkomera mtima.

23 Wosauka amadandaulira;Koma wolemera ayankha mwaukali.

24 Woyanjana ndi ambiri angodziononga;Koma liripo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31