15 Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;
16 Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.
17 Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;
18 Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.
19 Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,
20 Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;
21 Iitana posonkhana anthu polowera pacipata;M'mudzi inena mau ace;