19 Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,
20 Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;
21 Iitana posonkhana anthu polowera pacipata;M'mudzi inena mau ace;
22 Kodi mudzakonda zacibwana kufikira liti, acibwana inu?Onyoza ndi kukonda kunyoza,Opusa ndi kuda nzeru?
23 Tembenukani pamene ndikudzudzulani;Taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,Ndikudziwitsani mau anga.
24 Cifukwa ndaitana, ndipo munakana;Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;
25 Koma munapeputsa uphungu wangawonse,Ndi kukana kudzudzula kwanga.